Publicidade

Confiança

Por Bíblia Online

A confiança em Deus é âncora da alma em tempos de tempestade. Quem confia no Senhor não será abalado — porque o Deus fiel sustenta, protege e guia os que nele esperam.

Confiança inabalável

Tudo posso naquele que me fortalece. O meu Deus suprirá toda necessidade. Quem confia não será confundido.

Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.

Nanga tsono tidzanena chiyani pa izi? Ngati Mulungu ali mbali yathu, adzatitsutsa ife ndani?

ngakhale kutalika, kapena kuya, kapena chilichonse mʼchilengedwe chonse, sizingathe kutisiyanitsa ndi chikondi cha Mulungu chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba

adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.

Ndidzanena za Yehova, "Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,

Mulungu wanga amene ndimadalira."

Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

Fundamento de confiança

Deus não é homem para que minta. Todas as suas promessas são firmes. Confiar em Deus é segurança absoluta.

Mulungu si munthu kuti aname,

kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake.

Kodi amayankhula koma osachita?

Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?

Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati,

"Sadzakusiyani,

kapena kukutayani konse."

Kotero ife tikunena molimba mtima kuti,

"Ambuye ndiye mthandizi wanga;

sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?"

Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.

Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.

Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse

ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,

ndipo Iye adzawongola njira zako.

Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse

ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,

ndipo Iye adzawongola njira zako.

Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,

ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,

ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha,

koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.

Confiar em todas as coisas

Não pertenço ao mundo — minha cidadania é do céu. A confiança cristã repousa na fidelidade de Deus, não nas circunstâncias.

Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.

Yesu anati, " Ngati mungathe!Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira."

Yesu anayankha kuti, "Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu."

Onani mbalame zamlengalenga sizifesa kapena kukolola kapena kusunga mʼnkhokwe komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Kodi inu simuziposa kwambiri?

"Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi."

"Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova,

amene amatsamira pa Iye.

Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi

umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje.

Mtengowo suopa pamene kukutentha;

masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse.

Suchita mantha pa chaka cha chilala

ndipo sulephera kubereka chipatso."

Pamene ukuwoloka nyanja,

ndidzakhala nawe;

ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,

sidzakukokolola.

Pamene ukudutsa pa moto,

sudzapsa;

lawi la moto silidzakutentha.

Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.

Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.

Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife.

Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye.

Kuyesa Mizimu

Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi.

Esperar com confiança

O Senhor está perto de todos os que o invocam. Na espera confiante encontramos descanso e direção divina.

Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;

khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.

Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?

Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.

Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.

Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo.

Ife timakhala mwachikhulupiriro, osati mwa zooneka ndi maso.

Seja o primeiro
Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-