Falar
A Bíblia tem muito a ensinar sobre a arte de falar. As palavras têm poder de vida e de morte — podem edificar ou destruir, curar ou ferir, aproximar ou afastar.
O poder das palavras
A morte e a vida estão no poder da língua. A palavra branda desvia a ira, mas a palavra dura suscita o furor.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.
Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,
koma mawu ozaza amautsa ukali.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,
koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,
ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,
koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Falar com sabedoria
No muito falar não falta transgressão. A boca do justo fala sabedoria, e quem guarda os lábios guarda a si mesmo.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,
koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,
koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete;
ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;
koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.
Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa,
koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
Falar a verdade
Cada palavra ociosa será pesada no dia do juízo. Fale a verdade, edifique com a boca e confesse Cristo com os lábios.
Ine ndikukuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro munthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mawu aliwonse wopanda pake amene anayankhula.
"Ngati mʼbale wako akuchimwira, pita kamuwuze cholakwa chake pa awiri. Ngati akumvera, wamubweza mʼbale wakoyo.
Ndipo pamene mukupemphera, musamabwerezabwereza monga akunja, pakuti iwo amaganiza kuti adzamveka chifukwa chochulutsa mawu.
Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, "Yesu ndiye Ambuye," ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa.
Edificar com palavras
Não saia da boca nenhuma palavra torpe. Sejam prontos para ouvir, tardios para falar, e tardios para a ira.
Mʼkamwa mwanu musatuluke mawu aliwonse onyansa, koma okhawo amene ndi othandiza kulimbikitsa ena molingana ndi zosowa zawo, kuti athandize amene akawamve.
Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima.
Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.
Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso.
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake;
lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,
kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.