Publicidade

Ídolos

Por Bíblia Online

A Bíblia condena a idolatria com veemência. Um ídolo é qualquer coisa que ocupa o lugar de Deus no coração. Os cristãos são chamados a guardar-se dos ídolos e servir ao Deus vivo.

Guardai-vos dos ídolos

Filhinhos, guardai-vos dos ídolos. A cobiça é idolatria. Tudo que ocupa o trono de Deus no coração é um ídolo.

Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.

Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.

Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.

Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’ "

Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mu Igupto.

Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,

palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.

O único Deus verdadeiro

O Senhor é Deus nos céus e na terra — não há outro. Escolham hoje a quem servir, mas eu e a minha casa serviremos ao Senhor.

Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.

Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.

Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova."

Kodi simukudziwa kuti munthu woyipa sadzalowa mu ufumu wa Mulungu? Musanyengedwe: achigololo, kapena opembedza mafano, kapena achiwerewere, kapena amuna adama, kapena ogonana ndi amuna okhaokha; kapena akuba, kapena aumbombo, kapena oledzera, kapena achipongwe, kapena opeza ndalama mwachinyengo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu.

Vencer a idolatria

Não tenhas comunhão com as obras das trevas. Revesti-vos da armadura de Deus para resistir às ciladas do diabo.

Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse. Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.

Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana.

Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.

palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,

ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.

Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.

Chipambano chawo chichokera kwa Ine,"

akutero Yehova.

Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

funafuna mtendere ndi kuwulondola.

Ululu wa imfa ndi tchimo, ndipo mphamvu ya tchimo ndi lamulo.

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-22_10-02-25-