Publicidade

Meditação

Por Bíblia Online

A meditação na Palavra de Deus é prática espiritual essencial. Diferente da meditação oriental, a meditação bíblica é reflexão profunda sobre as Escrituras — ruminar a Palavra dia e noite.

Meditar na Palavra dia e noite

Bem-aventurado o homem que medita na lei do Senhor de dia e de noite. Ele é como árvore plantada junto a ribeiros de águas.

Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.

Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!

Ndimalingaliramo tsiku lonse.

Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,

popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.

Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse

popeza ndimalingalira umboni wanu.

Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,

popeza ndimamvera malangizo anu.

Ndimalingalira malangizo anu

ndipo ndimaganizira njira zanu.

Ndimakondwera ndi malamulo anu;

sindidzayiwala konse mawu anu.

Gimeli

popeza ndimakondwera ndi malamulo anu

chifukwa ndimawakonda.

Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,

ndipo ndimalingalira malangizo anu.

Zayini

Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;

chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.

Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,

kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.

Frutos da meditação

A meditação produz entendimento, alegria e adoração. Quem medita na Palavra encontra direção, paz e renovação espiritual.

Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;

Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.

Ndidzakumbukira ntchito zanu

ndi kulingalira zodabwitsa zanu."

Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,

ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.

Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;

ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.

Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,

pamene ndikusangalala mwa Yehova.

Seja o primeiro
Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-