Publicidade

A mulher virtuosa

Por Bíblia Online

A mulher virtuosa de Provérbios 31 é um retrato de excelência. Seu valor excede o de rubis — ela é sábia, trabalhadora, generosa e teme ao Senhor acima de tudo.

Uma joia rara

Mulher virtuosa, quem a achará? Seu valor excede o de rubis. Ela é o coração da família e a força do lar.

Mathero: Mkazi Wangwiro

Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?

Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.

Mathero: Mkazi Wangwiro

Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?

Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.

Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira

ndipo mwamunayo sasowa phindu.

Masiku onse a moyo wake

mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.

Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;

amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.

Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,

amakatenga chakudya chake kutali.

Iye amadzuka kusanache kwenikweni;

ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya

ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.

Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;

ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.

Iye amavala zilimbe

nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.

Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,

choncho nyale yake sizima usiku wonse.

Iye amadzilukira thonje

ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.

Iye amachitira chifundo anthu osauka

ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.

Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake,

koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.

Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.

Caráter acima da aparência

Enganosa é a graça e vã é a formosura, mas a mulher que teme ao Senhor será louvada. A verdadeira beleza é interior.

Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;

koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.

Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

Mkazi wanzeru amamanga banja lake,

koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo;

koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.

Chimodzimodzinso, phunzitsa amayi achikulire kuti akhale aulemu mʼmakhalidwe awo, asakhale osinjirira anzawo kapena zidakwa, koma akhale alangizi abwino. Tsono atha kulangiza amayi achichepere kukonda amuna awo ndi ana awo. Kuwaphunzitsa kukhala odziletsa ndi oyera mtima, osamala bwino mabanja awo, okoma mtima, ndi ogonjera amuna awo. Choncho palibe amene adzanyoze mawu a Mulungu.

Seja o primeiro
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-07-05_19-25-13-