Palavras de consolo
A Bíblia é repleta de palavras de consolo para os aflitos. Deus está perto dos que sofrem e promete enxugar toda lágrima, renovar a esperança e restaurar o coração partido.
Deus está conosco
O Senhor é refúgio e fortaleza. Mesmo no vale da sombra da morte, não precisamos temer — Ele está ao nosso lado para nos consolar.
Ngakhale ndiyende
mʼchigwa cha mdima wakuda bii,
sindidzaopa choyipa,
pakuti Inu muli ndi ine;
chibonga chanu ndi ndodo yanu
zimanditonthoza.
Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;
ndidzaopa yani?
Yehova ndi linga la moyo wanga;
ndidzachita mantha ndi yani?
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima,
linga pa nthawi ya mavuto.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,
ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:
kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova
masiku onse a moyo wanga,
ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,
ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Pakuti pa tsiku la msautso
Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;
adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake
ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Consolação e esperança
Deus consola os humildes e exalta os abatidos. Ele nunca nos desamparará.
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima."
Musawaope chifukwa Yehova Mulungu mwini adzakumenyerani nkhondo."
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite."
Iye amakweza anthu wamba,
ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino,
Descanso e renovação
Bem-aventurados os que choram, pois serão consolados. A Bíblia nos convida a descansar nos braços do Pai e encontrar paz para a alma.
Odala ndi amene ali achisoni,
chifukwa adzatonthozedwa.
Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni. Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu
kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,
pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha;
ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Chilichonse Chili ndi Nthawi
Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake,
ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:
Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira,
nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.
Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa,
nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.
Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala,
nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.
Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala,
nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.
Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna,
nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.
Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka,
nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.
Nthawi yokondana ndi nthawi yodana,
nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.