34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;
chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 Fuwulani kuti, "Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,
mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina,
kuti tiyamike dzina lanu loyera,
kuti tikutamandeni."
36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli,
kuyambira muyaya mpaka muyaya.
Ndipo anthu onse anati, "Ameni" ndipo "Tikutamandani Yehova."