Pular para o conteúdo
Publicidade

1 Pedro 1

23 Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. 24 Pakuti,

"Anthu onse ali ngati udzu,

ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo.

Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,

25 koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya."

Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu.

Veja também