Pular para o conteúdo
Publicidade

1 SAMUELI 16

11 Tsono Samueli anafunsa Yese kuti, "Kodi awa ndi ana ako onse aamuna?"

Yese anayankha kuti, "Ayi, alipo wina wamngʼono amene watsala, koma akuweta nkhosa."

Samueli anati, "Apite munthu akamutenge popeza sitipereka nsembe mpaka iye atabwera."

12 Choncho anatuma munthu kukamutenga ndipo anabwera naye. Iye anali wofiirira, wa maonekedwe abwino ochititsa kaso.

Ndipo Yehova anati, "Mudzoze popeza ndi ameneyu."

13 Samueli anatenga botolo la mafuta ndi kumudzoza pamaso pa abale ake, ndipo Mzimu wa Yehova unabwera mwamphamvu pa Davide kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo. Pambuyo pake Samueli anabwerera ku Rama.

Veja também