Za Kukhululukira Wolakwa
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera. 6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira. 7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima. 8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye.