5 "Mafunde a imfa anandizinga;
mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda;
misampha ya imfa inalimbana nane.
7 "Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;
ndinapemphera kwa Mulungu wanga.
Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga;
kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.