Buku la Mwana Wankhosa
1 Kenaka ndinaona buku mʼdzanja la wokhala pa mpando waufumu uja. Bukulo linali lolembedwa mbali zonse ndipo linali lomatidwa ndi zomatira zisanu ndi ziwiri. 2 Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti, "Ndani ali woyenera kumatula zomatira ndi kufutukula bukuli?"