Publicidade

Atos 2

Uthenga wa Petro

14 Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: "Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena. 15 Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa! 16 Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:

17 " Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza

ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.

Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera,

anyamata anu adzaona masomphenya,

nkhalamba zanu zidzalota maloto.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-