Pular para o conteúdo
Publicidade

MACHITIDWE A ATUMWI 2

17 " Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza

ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.

Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera,

anyamata anu adzaona masomphenya,

nkhalamba zanu zidzalota maloto.

18 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi,

ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo,

ndipo iwo adzanenera.

19 Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga

ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano,

ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.

20 Dzuwa lidzadetsedwa

ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi

lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.

21 Ndipo aliyense amene adzayitana

pa dzina la Ambuye adzapulumuka.

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também