42 Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti,
" ‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja
munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki
ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani,
mafano amene munapanga kuti muziwapembedza.
Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.