1 Uzikumbukira mlengi wako
masiku a unyamata wako,
masiku oyipa asanafike,
nthawi isanafike pamene udzanena kuti,
"Izi sizikundikondweretsa."
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala,
mwezi ndi nyenyezi zidzada.
Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera,
miyendo yako idzafowoka,
pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka,
ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.