8 Panali munthu amene anali yekhayekha;
analibe mwana kapena mʼbale.
Ntchito yake yolemetsa sinkatha,
ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.
Iye anadzifunsa kuti, "Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?
Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?"
Izinso ndi zopandapake,
zosasangalatsa!