23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, "Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa? 24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo? 25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?"
26 Yehova anati, "Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo."
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, "Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe, 28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?"
Iye anati, "Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga."
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, "Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?"
Iye anayankha, "Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero."
30 Ndipo Abrahamu anati, "Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?"
Iye anayankha, "Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu."
31 Abrahamu anati, "Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?"
Iye anati, "Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga."
32 Kenaka Abrahamu anati, "Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?"
Iye anayankha nati, "Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga."
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.