Pular para o conteúdo
Publicidade

GENESIS 3

17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, "Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, Usadye.

"Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19 Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera."

Veja também