Yosefe Adziwulula kwa Abale Ake
1 Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, "Aliyense achoke pamaso panga!" Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake. 2 Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
3 Yosefe anati kwa abale ake, "Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?" Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.