Ngʼambani Mtima Wanu
12 "Ngakhale tsopano,
bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse
posala zakudya ndi kukhetsa misozi," akutero Yehova.
13 Ngʼambani mtima wanu
osati zovala zanu.
Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu,
pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka,
ndipo amaleka kubweretsa mavuto.