27 Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza."
28 Kenaka anamufunsa Iye kuti, "Kodi tichite chiyani kuti tigwire ntchito za Mulungu?"
29 Yesu anayankha kuti, "Ntchito ya Mulungu ndi iyi: Kukhulupirira Iye amene anamutuma."