5 Yesu atakweza maso ndi kuona gulu lalikulu la anthu likubwera kwa Iye, anati kwa Filipo, "Kodi tingagule kuti buledi kuti anthu awa adye?" 6 Iye anafunsa izi kumuyesa chabe, pakuti Iye ankadziwa chimene ankayenera kuchita.
7 Filipo anamuyankha Iye kuti, "Malipiro a miyezi isanu ndi itatu sangathe kugula buledi okwanira aliyense kuti adye!"