Publicidade

Lucas 10

Fanizo la Msamariya Wachifundo

25 Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, "Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?"

26 Yesu anayankha kuti, "Mwalembedwa chiyani mʼMalamulo, ndipo iwe umawerenga zotani?"

27 Iye anayankha kuti, "Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse ndi nzeru zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini."

28 Yesu anayankha kuti, "Iwe wayankha bwino, chita zimenezi ndipo udzakhala ndi moyo."

29 Koma iye anafuna kudzilungamitsa yekha, ndipo anamufunsanso Yesu kuti, "Kodi mnansi wanga ndani?"

30 Yesu pomuyankha anati, "Munthu wina ankatsikira ku Yeriko kuchokera ku Yerusalemu. Pa njira anavulazidwa ndi achifwamba. Anamuvula zovala zake, namumenya ndi kuthawa, namusiya ali pafupi kufa. 31 Wansembe ankapita pa njira yomweyo, ndipo ataona munthuyo, analambalala. 32 Chimodzimodzinso, Mlevi wina pamene anafika pa malopo ndi kumuona, analambalalanso. 33 Koma Msamariya wina, ali pa ulendo wake, anafika pamene panali munthuyo; ndipo atamuona, anamva naye chisoni. 34 Anapita panali munthu wovulalayo, nathira mafuta ndi vinyo pa zilonda zake, nʼkuzimanga. Kenaka anamukweza pa bulu wake, napita naye ku nyumba ya alendo, namusamalira. 35 Mmawa mwake anatenga ndalama ziwiri zasiliva nazipereka kwa woyangʼanira nyumbayo, nati, Musamalireni munthuyu, ndipo pobwera ndidzakubwezerani zonse zimene mugwiritse ntchito.

36 "Kodi ukuganiza ndi ndani mwa atatuwa, amene anali mnansi wa munthu amene anavulazidwa ndi achifwambawo?"

37 Katswiri wa Malamulo uja anayankha kuti, "Amene anamuchitira chifundo."

Yesu anamuwuza kuti, "Pita, uzikachita chimodzimodzi."

Veja também

Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-07-05_19-25-13-