Pular para o conteúdo
Publicidade

Lucas 19

Zakeyu Apulumutsidwa

1 Yesu analowa mu Yeriko napitirira. 2 Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera. 3 Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu. 4 Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.

5 Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, "Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero." 6 Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.

7 Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, "Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa."

8 Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, "Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi."

9 Yesu anati kwa iye, "Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu. 10 Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho."

Veja também