Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi. 17 Yesu anati, "Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu." 18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.