Pular para o conteúdo
Publicidade

Marcos 10

4 Iwo anati, "Mose amaloleza mwamuna kulemba kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa mkazi."

5 Yesu anayankha kuti, "Mose anakulemberani lamulo ili chifukwa chakuwuma kwa mitima yanu. 6 Koma pachiyambi cha chilengedwe, Mulungu analenga iwo, mwamuna ndi mkazi. 7 Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, 8 ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.Potero sali awirinso, koma mmodzi. 9 Chifukwa chake chimene Mulungu wachilumikiza pamodzi, munthu wina asachilekanitse."

Veja também