22 Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, "Tengani, ili ndi thupi langa."
23 Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo.
24 Iye anawawuza kuti, "Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri. 25 Zoonadi, ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mphesa mpaka tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano mu ufumu wa Mulungu."