Amayi ndi Abale ake a Yesu
31 Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye. 32 Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, "Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani."
33 Iye anafunsa kuti, "Amayi ndi abale anga ndi ndani?"
34 Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, "Awa ndi amayi anga ndi abale anga! 35 Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga."