Pular para o conteúdo
Publicidade

MARKO 3

Amayi ndi Abale ake a Yesu

31 Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye. 32 Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, "Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani."

33 Iye anafunsa kuti, "Amayi ndi abale anga ndi ndani?"

34 Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, "Awa ndi amayi anga ndi abale anga! 35 Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga."

Estes versículos te tocaram? Ore agora!

+581 estão orando agora.

Junte-se à corrente de oração.

Veja também