Pular para o conteúdo
Publicidade

MATEYU 15

3 Yesu anayankha kuti, "Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu? 4 Pakuti Mulungu anati, Lemekeza abambo ako ndi amayi akondipo aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. 5 Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu, 6 iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu. 7 Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,

8 " Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

9 Amandilambira Ine kwachabe

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ "

Veja também