Petro Avomereza za Yesu
13 Yesu atafika ku chigawo cha Kaisareya Filipo, Iye anafunsa ophunzira ake kuti, "Kodi anthu amati Mwana wa Munthu ndi ndani?"
14 Iwo anayankha kuti, "Ena amati ndi Yohane Mʼbatizi; ena amati ndi Eliya; komanso ena amati Yeremiya kapena mmodzi wa aneneri."
15 Iye anafunsa kuti, "Nanga inuyo mumati ndine yani?"
16 Simoni Petro anayankha kuti, "Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo."