Publicidade

Mateus 18

Wamkulu mu Ufumu Wakumwamba

1 Pa nthawi imeneyo ophunzira anabwera kwa Yesu ndipo anamufunsa kuti, "Wamkulu woposa onse ndani mu ufumu wakumwamba?"

2 Iye anayitana kamwana kakangʼono ndi kukayimiritsa pakati pawo. 3 Ndipo Iye anati, "Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati simusintha ndi kukhala ngati tiana tatingʼono, simudzalowa konse mu ufumu wakumwamba. 4 Chifukwa chake, aliyense amene adzichepetsa yekha ngati kamwana aka, ameneyo ndiye wamkulu koposa onse mu ufumu wakumwamba.

Veja também

Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-07-04_21-26-40-