Pular para o conteúdo
Publicidade

Mateus 2

3 Mfumu Herode atamva zimenezi, anavutika mu mtima kwambiri pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu. 4 Ndipo anayitanitsa anthu onse, akulu ansembe ndi aphunzitsi amalamulo nawafunsa kuti, "Kodi Khristu adzabadwira kuti?" 5 Ndipo anamuyankha kuti, "Ku Betelehemu wa ku Yudeya chifukwa izi ndi zimene mneneri analemba kuti,

6 " Koma iwe Betelehemu, chigawo cha Yudeya,

sindiwe wamngʼonongʼono mwa olamulira a Yudeya;

pakuti otsogolera adzachokera mwa iwe,

amene adzaweta anthu anga Aisraeli.’ "

7 Pomwepo Herode anawayitanira mseri Anzeruwo nawafunsitsa nthawi yeniyeni yomwe nyenyeziyo inaoneka. 8 Ndipo anawatumiza ku Betelehemu nawawuza kuti, "Pitani mukafufuze za mwanayo mosamalitsa. Ndipo mukamupeza mudzandiwuze kuti inenso ndikamupembedze."

Veja também