15 Koma akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ataona zodabwitsa zimene anachita, komanso ana akufuwula mʼNyumbayo kuti, "Hosana kwa Mwana wa Davide," anapsa mtima.
16 Anamufunsa kuti, "Kodi mukumva zimene anawa akunena?"
Yesu anayankha nati, "Inde. Kodi simunawerenge kuti,
"Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda
mwatuluka mayamiko?"