Pular para o conteúdo
Publicidade

Mateus 4

Yesu Ayesedwa Mʼchipululu

1 Pambuyo pake Yesu anatsogozedwa ndi Mzimu Woyera kupita ku chipululu kukayesedwa ndi mdierekezi. 2 Ndipo atasala kudya masiku makumi anayi usana ndi usiku, anamva njala. 3 Woyesayo anadza kwa Iye nati, "Ngati ndinu mwana wa Mulungu, sandutsani miyala iyi kuti ikhale buledi."

4 Yesu anayankha kuti, "Zalembedwa, Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Mulungu.’ "

5 Pamenepo mdierekezi anapita naye ku mzinda woyera namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. 6 Ndipo anati, "Ngati ndinu Mwana wa Mulungu, dziponyeni nokha pansi. Pakuti kwalembedwa:

" Adzalamulira angelo ake za iwe,

ndipo adzakunyamula ndi manja awo

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.’ "

7 Yesu anamuyankha kuti, "Kwalembedwanso: Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ "

8 Kenaka mdierekezi anamutengera Yesu ku phiri lalitali kwambiri namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi ndi ulemerero wawo. 9 Ndipo anati kwa Iye, "Zonsezi ndidzakupatsani ngati mutandiweramira ndi kundipembedza ine."

10 Yesu anati kwa iye, "Choka Satana! Zalembedwa, Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ "

11 Pamenepo mdierekezi anamusiya ndipo angelo anamutumikira Iye.

Veja também