Za Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu
18 Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, "Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo." 19 Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.