Pular para o conteúdo
Publicidade

Mateus 9

2 Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, "Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa."

3 Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, "Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano."

4 Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, "Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu? 5 Chapafupi ndi chiti kunena kuti, Machimo ako akhululukidwakapena kunena kuti, Imirira ndipo yenda? 6 Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’ " 7 Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo.

Veja também