33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo. 34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti,
"Dzukani, Inu Yehova!
Adani anu abalalike;
Odana nanu athawe pamaso panu.
36 "Pamene likupumula, ankanena kuti,
"Bwererani, Inu Yehova,
ku chinamtindi cha Aisraeli."