Mathero: Mkazi Wangwiro
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?
Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira
ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Masiku onse a moyo wake
mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.