10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?
Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira
ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Masiku onse a moyo wake
mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;
amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,
amakatenga chakudya chake kutali.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;
ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya
ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;
ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Iye amavala zilimbe
nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,
choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Iye amadzilukira thonje
ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka
ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.