Publicidade

Provérbios 31

Mathero: Mkazi Wangwiro

10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?

Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.

11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira

ndipo mwamunayo sasowa phindu.

12 Masiku onse a moyo wake

mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.

13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;

amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.

14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,

amakatenga chakudya chake kutali.

15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;

ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya

ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.

16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;

ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.

17 Iye amavala zilimbe

nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.

18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,

choncho nyale yake sizima usiku wonse.

19 Iye amadzilukira thonje

ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.

20 Iye amachitira chifundo anthu osauka

ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.

Veja também

Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-07-05_19-25-13-