24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;
amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;
ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Iye amayankhula mwanzeru,
amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake
ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.