Nzeru Iposa Zonse
1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
Choncho musasiye malangizo anga.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
"Ugwiritse mawu anga pa mtima pako,
usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
Uziyikonda ndipo idzakuteteza.