5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.