Pular para o conteúdo
Publicidade

Provérbios 5

15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako,

madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.

16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu?

Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?

17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha,

osati uyigawireko alendo.

18 Yehova adalitse kasupe wako,

ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.

19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino.

Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse,

ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.

20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo?

Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?

Veja também