3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi.
Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu;
ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa;
akamayenda ndiye kuti akupita ku manda.
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo;
njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Tsopano ana inu, mundimvere;
musawasiye mawu anga.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo,
usayandikire khomo la nyumba yake,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena;
ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,