Pular para o conteúdo
Publicidade

Rute 1

8 Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, "Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.

9 "Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna." Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

10 Ndipo anati kwa Naomi, "Ife tipita nawo kwa anthu akwanu."

11 Koma Naomi anati, "Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu? 12 Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna, 13 kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike."

14 Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.

Veja também

Rute
Ver todos os capítulos de Rute