14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
tsiku la mdima ndi lachisoni,
tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
ndi nsanja za pa ngodya.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu
ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
sadzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
onse okhala pa dziko lapansi.