Publicidade

Ajuda

Por Bíblia Online

Deus é nosso auxílio e socorro em todo tempo. Ele não dorme nem cochila. O Senhor é nosso ajudador — não precisamos temer o que o homem possa nos fazer.

Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.

Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova;

Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.

Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa;

Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa,

pakuti amathawira kwa Iye.

Bwerani msanga kudzandithandiza,

Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;

tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu

chifukwa cha dzina lanu.

Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,

amene ndikukugwira dzanja lako lamanja

ndipo ndikuti, usaope;

ndidzakuthandiza.

Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso;

mumawerama kuti mundikweze.

"Idzani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo.

Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse.

Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa. Koma Iye amene amasanthula mitima yathu amadziwa maganizo a Mzimu, chifukwa Mzimu amapempherera oyera mtima molingana ndi chifuniro cha Mulungu.

Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse

ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,

ndipo Iye adzawongola njira zako.

Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.

Seja o primeiro
Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-