Publicidade

Gratidão

Por Bíblia Online

A gratidão é a resposta natural do coração que reconhece as bênçãos de Deus. A Bíblia transborda de exortações a dar graças — em tudo, por tudo, sempre e com todo o coração.

Dai graças em tudo

Em tudo dai graças, porque esta é a vontade de Deus em Cristo Jesus para convosco. A gratidão é mandamento, não opção.

Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

Kondwerani nthawi zonse. Pempherani kosalekeza. Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.

Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.

Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.

Malangizo Ena

Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika.

Malangizo Ena

Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika.

Gratidão como louvor

Entrai pelas portas com ação de graças e nos átrios com louvor. A gratidão é o perfume do louvor que sobe a Deus.

Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

Salimo. Nyimbo yothokoza.

Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

Mulambireni Yehova mosangalala;

bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.

Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.

Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.

Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;

kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;

tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;

Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.

Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,

ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse

chipulumutso cha Mulungu."

Reconhecer a Deus

Rendei graças ao Senhor porque Ele é bom. Sua misericórdia dura para sempre. Cada bênção é motivo de gratidão.

Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino.

Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;

chikondi chake chikhala mpaka muyaya.

Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;

chikondi chake chikhala mpaka muyaya.

Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.

Fuwulani kuti, "Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,

mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina,

kuti tiyamike dzina lanu loyera,

kuti tikutamandeni."

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,

ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya "Imfa ya Mwana." Salimo la Davide.

Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse;

ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.

Gratidão nas cartas apostólicas

Paulo sempre iniciava suas cartas com ação de graças a Deus pelos irmãos. A gratidão é essência da vida cristã.

ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.

Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu. Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.

Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu.

Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo.

Adzakulemeretsani pa zonse kuti mukhale owolowamanja pa nthawi zonse. Ndipo kuwolowamanja kwanu kudzera mwa ife, kudzakhala kuthokoza kwa Mulungu.

Adzakulemeretsani pa zonse kuti mukhale owolowamanja pa nthawi zonse. Ndipo kuwolowamanja kwanu kudzera mwa ife, kudzakhala kuthokoza kwa Mulungu.

Zonsezi nʼkuti inu mupindule, kuti chisomochi chifikire anthu ochuluka kwambiri, amenenso adzathokoza mochuluka kwambiri ndi kupereka ulemerero kwa Mulungu.

Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.

Agradecer a Deus

Graças a Deus que nos dá a vitória por nosso Senhor Jesus Cristo! A gratidão reconhece a fonte de toda boa dádiva.

Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.

Kuthokoza

Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu.

Kuyamika ndi Pemphero

Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe.

Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye.

Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni.

Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.

Pakuti chilichonse chimene Mulungu analenga ndi chabwino, ndipo chilichonse chisasalidwe, akamachilandira moyamika,

Louvor e ação de graças

Ofereçamos sacrifício de louvor e ação de graças ao Senhor. A gratidão é o coração de toda adoração verdadeira.

Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.

Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.

Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.

Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti,

"Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa,

kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu

mpaka muyaya!"

Iwo anati,

"Ameni!

Matamando ndi ulemerero,

nzeru, mayamiko, ulemu,

ulamuliro ndi mphamvu

zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi,

Ameni!"

Iwo anati,

"Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,

amene mulipo ndipo munalipo,

chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu,

ndipo mwayamba kulamulira.

Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.

Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga:

mwandipatsa nzeru ndi mphamvu,

mwandiwululira zomwe tinakupemphani,

mwatiwululira maloto a mfumu."

Imbirani Yehova ndi mayamiko;

imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.

Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga

ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,

kulengeza mofuwula za matamando anu

ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.

Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko

ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu.

Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo,

pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,"

akutero Ambuye Yehova.

Wolemekezeka Felike ife timazilandira zimenezi moyamika kwambiri ponseponse ndi mwa njira iliyonse.

Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova."

Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova."

Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova."

Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova

ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo.

Ndidzawachulukitsa,

ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika;

ndidzawapatsa ulemerero,

ndipo sadzanyozedwanso.

Malangizo Achipembedzo

Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.

Seja o primeiro
Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-