45 Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, "Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe."
46 Natanieli anafunsa kuti, "Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?"
Filipo anati, "Bwera udzaone."